Ishmael Thindwa wati sizoona kuti iye adakana kulowa mu Camp ya team ya dziko lino. Thindwa wati zomwe akunena mphuzitsi wa team ya dziko lino a Eddington Ng’onamo kuti Thindwa adakana kulowa mu Camp sizoona. Iye wati sangakane kukatumikira team ya dziko lake. Iye wati sadaitanidwe nawo ndipo wapempha mphuzitsi Eddington Ng’onamo asaiye kuuza atolankhani kuti iye adakana kulowa mu Camp ndipo wati iye amakhala okonzeka nthawi zonse kutumikira Malawi.

Subscribe to our Youtube Channel: