Apolisi aku Mozambique anjata asodzi aku Malawi kamba kowedza msomba m’nyanja ya Malawi ku gawo la Mozambique.

Asodzi pafupifupi makumi asanu ndi limodzi akumalawi ananjatidwa sabata latha  ndipo malipoti akuonetsa kuti asodziwa  anamasulidwa patapita masiku angapo potengere adindo aku  Malawi atafufuza zankhaniyi.

Koma maboti pafupifupi asanu ndi awiri sanabwezedwe ndi a polisi aku Mozambique.

Apolisi aku Mozambique anena kuti abweza ma botiwo pokhapokha asodiziwo apeleke k5 million kamba powedza  Nsomba popanda chilorezo ku gawo la Mozambique Mu nyanja ya Malawi.

Nyanja a Malawi ili mozunguliridwa ndi maiko a Mozambique ndi Tanzania ndipo nyanjayi maikowa anatengapo gawo pang’ono. Gawo laliku la nyanjali  lidatengedwa ndi dziko la Malawi.

Subscribe to our Youtube Channel: